24 Cifukwa ndaitana, ndipo munakana;Ndatambasula dzanja langa, ndipo panalibe analabadira;
25 Koma munapeputsa uphungu wangawonse,Ndi kukana kudzudzula kwanga.
26 Inetu ndidzacitiraciphwete tsoka lanu,Ndidzatonyola pakudza mantha anu;
27 Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.
28 Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;
29 Cifukwa anada nzeru,Sanafuna kuopa Yehova;
30 Anakana uphungu wanga,Nanyoza kudzudzula kwanga konse;