27 Pakudza mantha anu ngati mphepo yopasula,Ndi pofika tsoka lanu ngati kabvumvulu;Pakudza kwa inu bvuto ndi nsautso.
28 Pamenepo adzandiitana, koma sindidzabvomera;Adzandifunatu, osandipeza ai;
29 Cifukwa anada nzeru,Sanafuna kuopa Yehova;
30 Anakana uphungu wanga,Nanyoza kudzudzula kwanga konse;
31 Momwemo adzadya zipatso za mayendedwe ao,Nadzakhuta zolingalira zao.
32 Pakuti kubwerera m'mbuyo kwa acibwana kudzawapha;Ndipo mphwai za opusa zidzawaononga.
33 Koma wondimvera ine adzakhala osatekeseka,Nadzakhala phe osaopa zoipa,