7 Kuopa Yehova ndiko ciyambi ca kudziwa;Opusa anyoza nzeru ndi mwambo.
8 Mwananga, tamva mwambo wa atate wako,Ndi kusasiya cilangizo ca amako
9 Pakuti izi ndi korona wa cisomo pamtu pako,Ndi mkanda pakhosi pako.
10 Mwananga, akakukopa ocimwa usalole.
11 Akanena, Idza nafe, tibisalire mwazi,Tilalire osacimwa opanda cifukwa;
12 Tiwameze ali ndi moyo ngati manda,Ali amphumphu, ngati akutsikira kudzenje;
13 Tidzapeza cuma conse ca mtengo wace,Tidzadzaza nyumba zathu ndi zofunkha;