1 Mwana wanzeru akondweretsa atate;Koma mwana wopusa amvetsa amace cisoni.
2 Cuma ca ucimo sicithangata:Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.
3 Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;Koma amainga cifuniro ca wocimwa.
4 Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;Koma dzanja la akhama lilemeretsa.
5 Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.
6 Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
7 Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.