12 Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.
13 Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.
14 Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.
15 Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.
16 Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.
17 Wosunga mwambo ali m'njira ya moyo;Koma wosiya cidzudzulo asocera.
18 Wobisa udani ali ndi milomo yonama;Wonena ugogodi ndiye citsiru.