22 Madalitso a Yehova alemeretsa,Saonjezerapo cisoni.
23 Masewero a citsiru ndiwo kucita zoipa;Koma masewero a wozindikira ndiwo nzeru.
24 Comwe woipa aciopa cidzamfikira;Koma comwe olungama acifuna cidzapatsidwa.
25 Monga kabvumvulu angopita, momwemo woipa kuti zi;Koma olungama ndiwo maziko osatha.
26 Ngati vinyo wowawa m'mano, ndi utsi m'maso,Momwemo wolesi kwa iwo amene amtuma.
27 Kuopa Yehova kutanimphitsa masiku;Koma zaka za oipa zidzafinimpha,
28 Ciyembekezo ca olungama ndico cimwemwe;Koma cidikiro ca oipa cidzaonongeka.