6 Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
7 Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.
8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.
9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.
10 Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.
11 M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
12 Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.