8 Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.
9 Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.
10 Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.
11 M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
12 Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.
13 Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.
14 Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.