12 Wopeputsa mnzace asowa nzeru;Koma wozindikira amatonthola.
13 Kazitape woyendayenda amawanditsa zinsinsi;Koma wokhulupirika mtima abisa mau.
14 Popanda upo wanzeru anthu amagwa;Koma pocuruka aphungu pali cipulumutso.
15 Woperekera mlendo cikole adzaphwetekwapo;Koma wakuda cikole akhala ndi mtendere.
16 Mkazi wodekha agwiritsa ulemu;Aukali nagwiritsa cuma.
17 Wacifundo acitira moyo wace zokoma;Koma wankhanza abvuta nyama yace.
18 Woipa alandira malipiro onyenga;Koma wofesa cilungamo aonadi mphotho,