20 Okhota mtima anyansa Yehova;Koma angwiro m'njira zao amsekeretsa.
21 Zoonadi, wocimwa sadzapulumuka cilango;Koma mbeu ya olungama idzalanditsidwa.
22 Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.
23 Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.
24 Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.
25 Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.
26 Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.