22 Monga cipini cagolidi m'mphuno ya nkhumba,Momwemo mkazi wokongola wosasinkhasinkha bwino.
23 Cifuniro ca olungama cifikitsa zabwino zokha;Koma ciyembekezo ca oipa mkwiyo.
24 Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.
25 Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.
26 Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.
27 Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.
28 Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.