24 Alipo wogawira, nangolemerabe;Aliponso womana comwe ayenera kupatsa nangosauka.
25 Mtima wa mataya udzalemera;Wothirira madzi nayenso adzathiriridwa.
26 Womana tirigu anthu amtemberera;Koma madalitso adzakhala pamtu pa wogulitsa.
27 Wopwaira ubwino afunitsa cikondwerero;Koma zoipa zidzamfikira wozilondola.
28 Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.
29 Wobvuta banja lace adzalowa m'zomsautsa;Wopusa adzatumikira wanzeru.
30 Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo;Ndipo wokola mtima ali wanzeru.