28 Wokhulupmra cuma cace adzagwa;Koma olungama adzaphuka ngati tsamba.
29 Wobvuta banja lace adzalowa m'zomsautsa;Wopusa adzatumikira wanzeru.
30 Cipatso ca wolungama ndi mtengo wa moyo;Ndipo wokola mtima ali wanzeru.
31 Taonani, wolungama adzalandira mphotho kunja kuno;Koposa kotani woipa ndi wocimwa?