5 Cilungamo ca wangwiro cimaongola njira yace;Koma woipa adzagwa ndi zoipa zace.
6 Cilungamo ca oongoka mtima cidzawapulumutsa;Koma aciwembu adzagwidwa ndi mphulupulu yao.
7 Pomwalira woipa cidikiro cace cionongeka;Ciyembekezo ca ucimo cionongeka.
8 Wolungama apulumuka kubvuto;Woipa nalowa m'malo mwace.
9 Wonyoza Mulungu aononga mnzace ndi m'kamwa mwace;Koma olungama adzapulumuka pakudziwa,
10 Olungama akapeza bwino, mudzi usekera;Nupfuula pakuonongeka oipa.
11 Madalitso a olungama akuza mudzi;Koma m'kamwa mwa oipa muupasula.