12 Woipa akhumba cokodwa ndi amphulupulu;Koma muzu wa olungama umabala zipatso.
13 M'kulakwa kwa milomo muli msampha woipa;Koma wolungama amaturuka m'mabvuto.
14 Munthu amakhuta zabwino ndi zipatso za m'kamwa mwace;Zocita za manja ace zidzabwezedwa kwa iye.
15 Njira ya citsiru nlolungama pamaso pace pace;Koma wanzeru amamvera uphungu.
16 Mkwiyo wa citsiru udziwika posacedwa;Koma wanzeru amabisa manyazi.
17 Wolankhula ntheradi aonetsa cilungamo;Koma mboni yonama imanyenga.
18 Alipo wonena mwansontho ngati kupyoza kwa lupanga;Koma lilime la anzeru lilamitsa.