10 Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.
11 Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.
12 Ciyembekezo cozengereza cidwalitsa mtima;Koma pakufika cifuniroco ndico mtengo wa moyo.
13 Wonyoza mau adziononga yekha;Koma woopa malangizo adzalandira mphotho.
14 Malamulo a wanzeru ndiwo kasupe wa moyo,Apatutsa ku misampha ya imfa.
15 Nzeru yabwino ipatsa cisomo;Koma njira ya aciwembu iri makolokoto.
16 Yense wocenjera amacita mwanzeru:Koma wopusa aonetsa utsiru.