5 Wolungama ada mau onama;Koma woipa anyansa, nadzicititsa manyazi,
6 Cilungamo cicinjiriza woongoka m'njira;Koma udio ugwetsa wocimwa.
7 Alipo wodziyesa wolemera, koma alibe kanthu;Alipo wodziyesa wosauka, koma ali ndi cuma cambiri.
8 Ciombolo ca moyo wa munthu ndico cuma cace;Koma wosauka samva cidzudzulo.
9 Kuunika kwa olungama kukondwa;Koma nyali ya oipa idzazima.
10 Kudzikuza kupikisanitsa;Koma omwe anauzidwa uphungu ali ndi nzeru.
11 Cuma colandiridwa mokangaza cidzacepa;Koma wokundika ndi dzanja adzaona zocuruka.