1 Mayankhidwe ofatsa abweza mkwiyo;Koma mau owawitsa aputa msunamo.
2 Lilime la anzeru linena bwino zomwe adziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mutsanulira utsiru.
3 Maso a Yehova ali ponseponse,Nayang'anira oipa ndi abwino.
4 Kuciza lilime ndiko mtengo wa moyo;Koma likakhota liswa moyo.