11 Kumanda ndi kucionongeko kuli pamaso pa Yehova;Koposa kotani nanga mitima ya ana a anthu?
12 Wonyoza sakonda kudzudzulidwa,Samapita kwa anzeru.
13 Mtima wokondwa usekeretsa nkhope;Koma moyo umasweka ndi zowawa za m'mtima.
14 Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15 Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16 Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17 Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.