14 Mtima wa wozindikira ufunitsa kudziwa;Koma m'kamwa mwa opusa mudya utsiru.
15 Masiku onse a wosauka ali oipa;Koma wokondwera mtima ali ndi phwando losatha.
16 Zapang'ono, ulikuopa Yehova,Zipambana ndi katundu wambiri pokhala phokoso,
17 Kudya masamba, pali cikondano,Kuposa ng'ombe yonenepa pali udani.
18 Munthu wozaza aputa makani;Koma wosakwiya msanga atonthoza makangano.
19 Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.
20 Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.