19 Mayendedwe a wolesi akunga Hnga laminga,Koma njira ya oongoka mtima iundidwa ngati mseu.
20 Mwana wanzeru akondweretsa atate wace;Koma munthu wopusa apeputsa amace.
21 Wosowa nzeru akondwera ndi utsiru;Koma munthu wozindikira aongola mayendedwe ace.
22 Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23 Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,