22 Zolingalira zizimidwa popanda upoKoma pocuruka aphungu zikhazikika.
23 Munthu akondwera ndi mayankhidwe a m'kamwa mwace;Ndi mau a pa nthawi yace kodi sali abwino?
24 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,
26 Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.
27 Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.
28 Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.