24 Anzeru ayesa njira yamoyo yokwerakwera,Kuti apambuke kusiya kunsi kwa manda.
25 Yehova adzapasula nyumba ya wonyada;Koma adzalembera mkazi wamasiye malire ace,
26 Ziwembu zoipa zinyansa Yehova;Koma oyera mtima alankhula mau okondweretsa.
27 Wopindula monyenga abvuta nyumba yace;Koma wakuda mitulo adzakhala ndi moyo.
28 Mtima wa wolungama uganizira za mayankhidwe;Koma m'kamwa mwa ocimwa mutsanulira zoipa.
29 Yehova atarikira oipa;Koma pemphero la olungama alimvera.
30 Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima;Ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.