13 Wobwezera mau asanamvetse apusa,Nadzicititsa manyazi.
14 Mtima wa munthu umlimbitsa alikudwala;Koma ndani angatukule mtima wosweka?
15 Mtima wa wozindikira umaphunzira;Khutu la anzeru lifunitsa kudziwa.
16 Mtulo wa munthu umtsegulira njira,Numfikitsa pamaso pa akuru.
17 Woyamba kudzinenera ayang'anika wolungama;Koma mnzace afika namuululitsa zace zonse.
18 Ula uletsa makangano,Nulekanitsa amphamvu.
19 Kupembedza mbale utamcimwira nkobvuta,Kulanda mudzi wolimba nkosabvuta;Makangano akunga mipiringidzo ya linga.