21 Lilime liri ndi mphamvu pa imfa ndi moyo;Wolikonda adzadya zipatso zace.
22 Wopeza mkazi apeza cinthu cabwino;Yehova amkomera mtima.
23 Wosauka amadandaulira;Koma wolemera ayankha mwaukali.
24 Woyanjana ndi ambiri angodziononga;Koma liripo bwenzi lipambana ndi mbale kuumirira.