23 Kuopa Yehova kupatsa moyo;Wokhala nako adzakhala wokhuta;Zoipa sizidzamgwera.
24 Wolesi alonga dzanja lace m'mbale,Osalibwezanso kukamwa kwace.
25 Menya wonyoza, ndipo acibwana adzaceniera;Nudzudzule wozindikira adzazindikira nzeru.
26 Wolanda za atate, ndi wopitikitsa amai,Ndiye mwana wocititsa manyazi ndi wogwetsa nkhope.
27 Ukangofuna, mwananga, kusocera kusiya mau akudziwitsa,Leka kumva mwambo.
28 Mboni yopanda pace inyoza ciweruzo;M'kamwa mwa amphulupulu mumeza zoipa,
29 Akonzera onyoza ciweruzo,Ndi mikwingwirima pamsana pa opusa.