10 Miyeso yosiyana, ndi malicero osiyana,Zonse ziwirizi zinyansa Yehova.
11 Ngakhale mwana adziwika ndi nchito zace;Ngati nchito yace iri yoyera ngakhale yolungama.
12 Khutu lakumva, ndi diso lopenya,Yehova anapanga onse awiriwo.
13 Usakonde tulo ungasauke;Phenyula maso, udzakhuta zakudya.
14 Wogula ati, Cacabe cimeneco.Koma atacoka adzitama.
15 Alipo golidi ndi ngale zambiri;Koma milomo yodziwa ndiyo cokometsera ca mtengo wapatari.
16 Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi wacilendo cikole umgwire mwini.