1 Mtima wa mfumu uli m'dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi;Aulozetsa komwe afuna.
2 Njira zonse za munthu zilungama pamaso pace;Koma Yehova ayesa mitima.
3 Kucita cilungamo ndi ciweruzoKupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.
4 Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza,Ndi nyali ya oipa, ziri cimo.
5 Zoganizira za wakhama zicurukitsadi katundu;Koma yense wansontho angopeza umphawi.