12 Wolungama aganizira za nyumba ya wamphulupulu,Kuti amphulupulu amagwetsedwa, naona zoipa.
13 Wotseka makutu ace polira waumphawi,Nayenso adzalira koma osamvedwa.
14 Mphatso ya m'tseri ipembedza mkwiyo,Ndi mtulo wa pamfunga ukali wolimba.
15 Kucita ciweruzo kukondweretsa wolungama;Koma kuwaononga akucita mphulupulu,
16 Munthu wosocera pa njira ya nzeruAdzakhala m'msonkhano wa akufa.
17 Wokonda zoseketsa adzasauka;Wokonda vinyo ndi mafuta sadzalemera.
18 Wocimwa ndiye ciombolo ca wolungama;Ndipo waciwembu adzalowa m'malo mwa oongoka mtima.