11 Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.
12 Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.
13 Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.
14 Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.
15 Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;
16 Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.
17 Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;