13 Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.
14 Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.
15 Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;
16 Imso zanga zidzasangalala,Polankhula milomo yako zoongoka.
17 Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;
18 Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
19 Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.