2 Nuike mpeni pakhosi pako,Ngati uli wadyera.
3 Usakhumbe zolongosoka zace;Pokhala zakudya zonyenga.
4 Usadzitopetse kuti ulemere;Leka nzeru yako yako.
5 Kodi upenyeranji cimene kulibe?Pakuti cuma cunera mapiko,Ngati mphungu youluka mumlengalenga.
6 Usadye zakudya zace za wa maso ankhwenzule,Ngakhale kukhumba zolongosoka zace;
7 Pakuti monga asinkha m'kati mwace, ali wotere;Ati kwa iwe, Idya numwe;Koma mtima wace suli pa iwe.
8 Pakuti nthongo imene unaidya udzaisanza,Ndi kutaya mau ako okondweretsa.