20 Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.
21 Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.
22 Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.
23 Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.
24 Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.
25 Atate wako ndi amako akondwere,Amako wakukubala asekere.
26 Mwananga, undipatse mtima wako,Maso ako akondwere ndi njira zanga,