9 Usalankhule m'makutu a wopusa;Pakuti adzapeputsa nzeru ya mau ako.
10 Usasunthe cidziwitso cakale ca m'malire;Ngakhale kulowa m'minda ya amasiye;
11 Pakuti Mombolo wao walimba;Adzawanenera mlandu wao pa iwe.
12 Lozetsa mtima wako kumwambo,Ndi makutu ako ku mau a nzeru.
13 Usamane mwana cilango;Pakuti ukammenya ndi ntyole safa ai.
14 Udzammenya ndi ntyole,Nudzapulumutsa moyo wace kunsi kwa manda.
15 Mwananga, mtima wako ukakhala wanzeru,Mtima wanga wa inedi udzakondwa;