14 Potero udzadziwa kuti nzeru iri yotero m'moyo wako;Ngati waipeza padzakhala mphotho,Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
15 Usabisalire, woipa iwe, pomanga wolungama;Usapasule popuma iyepo.
16 Pakuti wolungama amagwa kasanu ndi kawiri, nanyamukanso;Koma oipa akhumudwa pomfikira tsoka.
17 Usakondwere pakugwa mdani wako;Mtima wako usasekere pokhumudwa iye;
18 Kuti Yehova angaone kukondwa kwako, ndi kukuyesa koipa,Ndi kuleka kumkwiyira.
19 Usabvutike mtima cifukwa ca ocita zoipa;Ngakhale kucitira nsanje amphulupulu;
20 Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.