20 Pakuti woipayo sadzalandira mphotho;Nyali ya amphulupulu idzazima.
21 Mwananga, opa Yehova ndi mfumu yomwe,Osadudukira anthu osinthasintha.
22 Pakuti tsoka lao lidzaoneka modzidzimuka;Ndipo ndani adziwa cionongeko ca zaka zao?
23 Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.
24 Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,
25 Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.
26 Wobwezera mau oongokaApsompsona milomo.