24 Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,
25 Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.
26 Wobwezera mau oongokaApsompsona milomo.
27 Longosola nchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda;Pambuyo pace ndi kumanga nyumba yako.
28 Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa;Kodi udzanyenga ndi milomo yako?
29 Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine;Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.
30 Ndinapita pa munda wa wolesi,Polima mphesa munthu wosowa nzeru.