1 Iyinso ndiyo miyambo ya SolomoImene anthu a Hezekiya mfumu ya Yuda anailemba.
2 Kubisa kanthu ndi ulemerero wa Mulungu;Koma ulemerero wa mafumu ndi kusanthula kanthu.
3 Pamlengalenga patarika, ndi padziko pakuya,Koma mitima ya mafumu singasanthulike.
4 Cotsera siliva mphala yace,Mmisiri wa ng'anjo aturutsamo mbale;
5 Cotsera woipa pamaso pa mfumu,Mpando wace udzakhazikika m'cilungamo.
6 Usadzitame pamaso pa mfumu,Ngakhale kuima m'malo mwa akuru;