12 Monga phelele lagolidi ndi cipini cagolidi woyengeka,Momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.
13 Monga cisanu ca cipale cofewa pa nthawi ya masika,Momwemo mthenga wokhulupirika kwa amene anamtuma;Atsitsimutsa moyo wa ambuyace.
14 Monga mitambo ndi mphepo popanda mvula,Momwemo ndiye wodzikweza ndi zipatso zace monyenga.
15 Cipiriro cipembedza mkuru;Lilime lofatsa lityola pfupa,
16 Wapeza uci kodi? Idyapo wokwanira,Kuti ungakukole, nusanze.
17 Phazi lako lilowe m'nyumba ya mnzako kamodzi kamodzi;Kuti angatope nawe ndi kukuda.
18 Wocitira mnzace umboni wonamaNdiye cibonga, ndi lupanga, ndi mubvi wakuthwa.