3 Pamlengalenga patarika, ndi padziko pakuya,Koma mitima ya mafumu singasanthulike.
4 Cotsera siliva mphala yace,Mmisiri wa ng'anjo aturutsamo mbale;
5 Cotsera woipa pamaso pa mfumu,Mpando wace udzakhazikika m'cilungamo.
6 Usadzitame pamaso pa mfumu,Ngakhale kuima m'malo mwa akuru;
7 Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno,Kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga,Amene maso ako anamuona.
8 Usaturuke mwansontho kukalimbana,Ungalephere pa kutha kwace,Atakucititsa mnzako manyazi.
9 Nena mlandu wako ndi mnzako,Osaulula zinsinsi za mwini;