6 Usadzitame pamaso pa mfumu,Ngakhale kuima m'malo mwa akuru;
7 Pakuti kunena kwa iwe, Takwera kuno,Kupambana ndi kuti utsitsidwe pamaso pa kalonga,Amene maso ako anamuona.
8 Usaturuke mwansontho kukalimbana,Ungalephere pa kutha kwace,Atakucititsa mnzako manyazi.
9 Nena mlandu wako ndi mnzako,Osaulula zinsinsi za mwini;
10 Kuti wakumva angakutonze,Mbiri yako yoipa ndi kusacoka.
11 Mau oyenera a pa nthawi yaceAkunga zipatso zagolidi m'nsengwa zasiliva.
12 Monga phelele lagolidi ndi cipini cagolidi woyengeka,Momwemo wanzeru wodzudzula pa khutu lomvera.