19 Momwemo wonyenga mnzace ndi kuti, Ndi kusewera kumeneku.
20 Posowa nkhuni moto ungozima;Ndi popanda kazitape makangano angoleka.
21 Monga makala ozizira pa makala akunyeka, ndi nkhuni pamoto;Momwemo munthu wamakangano autsa ndeu.
22 Mau a kazitape ndi zakudya zolongosokaZitsikira m'kati mwa mimba.
23 Milomo yofunitsitsa ndi mtima woipaIkunga mbale yadothi anaimata ndi mphala yasiliva.
24 Wakuda mnzace amanyenga ndi milomo yace;Koma akundika cinyengo m'kati mwace;
25 Pamene akometsa mau ace usamkhulupirire;Pakuti m'mtima mwace muli zonyansa zisanu ndi ziwiri.