11 Mwananga, khala wanzeru, nukondweretse mtima wanga;Kuti ndimuyankhe yemwe anditonza.
12 Wocenjera aona zoipa, nabisala;Koma acibwana angopitirira, nalipitsidwa.
13 Tenga maraya a woperekera mlendo cikole;Woperekera mkazi waciwerewere cikole umgwire mwini.
14 Yemwe adalitsa mnzace ndi mau akuru pouka mamawa,Anthu adzaciyesa cimeneco temberero.
15 Kudonthadontha tsiku lamvula,Ndi mkazi wolongolola ali amodzimodzi.
16 Wofuna kumletsayo afuna kuletsa mphepo;Dzanja lace lamanja lingogwira mafuta.
17 Citsulo cinola citsulo;Comweco munthu anola nkhope ya mnzace.