15 Monga mkango wobangula ndi cirombo coyendayenda,Momwemo mfumu yoipa ya anthu osauka.
16 Kalonga wosowa nzeru apambana kusautsa;Koma yemwe ada cisiriro adzatanimphitsa moyo wace.
17 Woparamula mlandu wakupha munthu adzathawira kudzenje;Asamuletse.
18 Woyenda mwangwiro adzapulumuka;Koma wokhota m'mayendedwe ace adzagwa posacedwa.
19 Wolima munda wace zakudya zidzamkwanira;Koma wotsata anthu opanda pace umphawi udzamkwanira.
20 Munthu wokhulupirika ali ndi madalitso ambiri;Koma wokangaza kulemera sadzapulumuka cilango,
21 Cetera siliri labwino,Ngakhale kulakwa kuti ukadye kanthu.