10 Anthu ankhanza ada wangwiro;Koma oongoka mtima asamalira moyowace.
11 Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.
12 Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,
13 Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.
14 Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15 Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.
16 Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.