14 Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15 Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.
16 Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.
17 Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.
18 Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.
19 Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.
20 Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.