1 Mwananga, usaiwale malamulo anga,Mtima wako usunge malangizo anga;
2 Pakuti adzakuonjezera masiku ambiri,Ndi zaka za moyo ndi mtendere.
3 Cifundo ndi coonadi zisakusiye;Uzimange pakhosi pako;Uzilembe pamtima pako;
4 Motero udzapezakisomo ndi nzeru yabwino,Pamaso pa Mulungu ndi anthu.
5 Khulupirira Yehova ndi mtima wako wonse,Osacirikizika pa luntha lako;