11 Mwananga, usapeputse mwambo wa Yehova,Ngakhale kutopa ndi kudzudzula kwace;
12 Pakuti Yehova adzudzula omwe awakonda;Monga atate mwana amene akondwera naye.
13 Wodala ndi wopeza nzeru,Ndi woona luntha;
14 Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.
15 Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.
16 Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.
17 Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.