14 Pakuti malonda a nzeru aposa malonda a siliva,Phindu lace liposa golidi woyengeka.
15 Mtengo wace uposa ngale;Ndipo zonse zikukondweretsa sizilingana naye.
16 Masiku ambiri ali m'dzanja lamanja lace;Cuma ndi ulemu m'dzanja lace lamanzere.
17 Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.
18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.
19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.
20 Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.