17 Njira zace ziri zokondweretsa,Mayendedwe ace onse ndiwo mtendere.
18 Ndiyo mtengo wa moyo wa akuigwira;Wakulumirira ngwodala.
19 Yehova anakhazika dziko ndi nzeru;Naika zamwamba ndi luntha.
20 Zakuya zinang'ambika ndi kudziwakwace;Thambo ligwetsa mame.
21 Mwananga, zisacokere ku maso ako;Sunga nzeru yeniyeni ndi kulingalira;
22 Ndipo mtima wako udzatengapo moyo,Ndi khosi lako cisomo.
23 Pompo udzayenda m'njira yako osaopa,Osapunthwa phazi lako.